The Rest of Daniel Chapter 13 13
Chapters: 13
The Rest of Daniel Chapter 13 Chapter 13
| Verse | English | Coptic | Dutch | French | German | Spanish | Italian | Turkish | Simplified Chinese | Traditional Chinese | Portuguese | Indonesian | Thai | Hindi | Chichewa | Urdu | Arabic |
|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|---|
| 13:1 | There was a man living in Babylon whose name was Joakim. | Ⲛⲉ ⲟⲩⲟⲛ ⲟⲩⲣⲱⲙⲓ ⲇⲉ ⲉϥϣⲟⲡ ϧⲉⲛ Ⲃⲁⲃⲩⲗⲱⲛ ⲉ̀ⲡⲉϥⲣⲁⲛ ⲡⲉ Ⲓⲱⲁⲕⲓⲙ. | Ku Babiloni kudaali munthu wina dzina lake Yowakimu. | ||||||||||||||
| 13:2 | He married the daughter of Hilkiah, named Susanna, a very beautiful woman and one who feared the Lord. | Ⲁϥϭⲓ ⲇⲉ ⲛ̀ⲟⲩⲥ̀ϩⲓⲙⲓ ⲉ̀ⲡⲉⲥⲣⲁⲛ ⲡⲉ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲧ̀ϣⲉⲣⲓ ⲛ̀Ⲭⲁⲗⲕⲓⲁⲥ ⲛⲉ ⲉⲛⲁⲛⲉⲥ ⲉⲙⲁϣⲱ ⲡⲉ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲥⲉⲣϩⲟϯ ϧⲁⲧϩⲏ ⲙ̀Ⲫϯ. | Adaakwatira mkazi wokongola kwambiri ndi woopa Mulungu, dzina lake Suzana, mwana wa Hilikiya. | ||||||||||||||
| 13:3 | Her parents were righteous, and had trained their daughter according to the law of Moses. | Ⲟⲩⲟϩ ⲛⲉⲥⲓⲟϯ ⲛⲉ ϩⲁⲛⲑ̀ⲙⲏⲒ ⲛⲉ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲩϯⲥ̀ⲃⲱ ⲛ̀ⲧⲟⲩϣⲉⲣⲓ ⲕⲁⲧⲁ ⲫ̀ⲛⲟⲙⲟⲥ ⲙ̀Ⲙⲱⲩ̀ⲥⲏⲥ ⲡⲉ. | Makolo a Suzana anali Ayuda oopa Mulungu, ndipo mwana waoyo adaamlera motsata malamulo a Mose. | ||||||||||||||
| 13:4 | Joakim was very rich, and had a fine garden adjoining his house; the Jews used to come to him because he was the most honored of them all. | Ⲓⲱⲁⲕⲓⲙ ⲇⲉ ⲛⲉ ⲟⲩⲣⲁⲙⲁⲟ̀ ⲡⲉ ⲉⲙⲁϣⲱ ⲛⲉ ⲟⲩⲟⲛⲧⲁϥ ⲙ̀ⲙⲁⲩ ⲛ̀ⲟⲩⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲉϥⲭⲏ ϧⲁⲑⲟⲩⲟϥ ⲙ̀ⲡⲉϥⲏⲓ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲩⲛⲏⲟⲩ ϩⲁⲣⲟϥ ⲧⲏⲣⲟⲩ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲓⲒⲟⲩⲇⲁⲓ ⲉⲑⲃⲉ ϫⲉ ⲛ̀ⲑⲟϥ ⲛⲁϥⲧⲁⲓⲏⲟⲩⲧ ⲉϩⲟⲧⲉ ⲉ̀ⲣⲱⲟⲩ ⲧⲏⲣⲟⲩ. | Yowakimu anali munthu wolemera kwambiri, ndipo anali ndi dimba labwino la mitengo pakhomo pake. Ayuda ankakumana kumeneko kaŵirikaŵiri, chifukwa iye anali munthu wotchuka kupambana iwo onse. | ||||||||||||||
| 13:5 | That year two elders from the people were appointed as judges. Concerning them the Lord had said: Wickedness came forth from Babylon, from elders who were judges, who were supposed to govern the people. | Ⲁⲩⲟⲩⲱⲛϩ ⲇⲉ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲛ̀ϫⲉ ⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥⲃ̅ ⲛ̀ⲣⲉϥϯϩⲁⲡ ⲉ̀ⲃⲟⲗϧⲉⲛ ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ϧⲉⲛ ϯⲣⲟⲙⲡⲓ ⲉⲧⲉⲙ̀ⲙⲁⲩ ⲛⲏⲉⲧⲁϥⲥⲁϫⲓ ⲉⲑⲃⲏⲧⲟⲩ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲉⲛⲛⲏⲃ ϫⲉ ⲁⲥⲓ̀ ⲛ̀ϫⲉ ⲟⲩⲁ̀ⲛⲟⲙⲓⲁ̀ ⲉ̀ⲃⲟⲗϧⲉⲛ Ⲃⲁⲃⲩⲗⲱⲛ ⲉ̀ⲃⲟⲗϧⲉⲛ ϩⲁⲛⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥ ⲛ̀ⲕ̀ⲣⲓⲧⲏⲥ ⲛⲁⲓ ⲉ̀ⲛⲁⲩⲙⲉⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲣⲱⲟⲩ ϫⲉ ⲥⲉⲉⲣϩⲉⲙⲓ ⲙ̀ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ. | Chaka chimenecho akuluakulu ena aŵiri adaasankhidwa kuti akhale aweruzi. Ponena za iwowo Ambuye adati, “Zoipa zidachokera ku Babiloni kwa akuluakulu oweruza amene akadayenera kuŵaongolera bwino anthu anga.” | ||||||||||||||
| 13:6 | These men were frequently at Joakim's house, and all who had a case to be tried came to them there. | Ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲓ ⲉ̀ϣⲁⲩⲑⲱⲟⲩϯ ⲉ̀ⲡ̀ⲏⲓ ⲛ̀Ⲓⲱⲁⲕⲓⲙ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲩⲑⲱⲟⲩϯ ϩⲁⲣⲱⲟⲩ ⲡⲉ ⲛ̀ϫⲉ ⲟⲩⲟⲛ ⲛⲓⲃⲉⲛ ⲉⲑϭⲓϩⲁⲡ. | Anthu aŵiriwo ankakhala nawo kunyumba kwa Yowakimu kaŵirikaŵiri, ndipo aliyense amene anali ndi mlandu ankabwera kwa iwo. | ||||||||||||||
| 13:7 | When the people left at noon, Susanna would go into her husband's garden to walk. | Ⲉϣⲱⲡ ⲁϥϣⲁⲛⲙⲟϣⲓ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ϧⲉⲛ ⲧ̀ⲫⲁϣⲓ ⲙ̀ⲡⲓⲉ̀ϩⲟⲟⲩ ϣⲁⲥⲓ̀ ⲉ̀ϧⲟⲩⲛ ⲛ̀ϫⲉ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲉⲥⲙⲟϣⲓ ϧⲉⲛ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲛ̀ⲧⲉ ⲡⲉⲥϩⲁⲓ. | Anthu onse atapita kukadya chakudya chamasana, Suzana uja ankayenda ku dimba la mwamuna wake. | ||||||||||||||
| 13:8 | Every day the two elders used to see her, going in and walking about, and they began to lust for her. | Ⲛⲁⲩϯⲛⲓⲁ̀ⲧⲟⲩ ⲙ̀ⲙⲟⲥ ⲙ̀ⲙⲏⲛⲓ ⲡⲉ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥ ⲉⲥⲛⲏⲟⲩ ⲉ̀ϧⲟⲩⲛ ⲉⲥⲙⲟϣⲓ ϧⲉⲛ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲁⲩϣⲱⲡⲓ ϧⲉⲛ ⲧⲉⲥⲉ̀ⲡⲓⲑⲩⲙⲓⲁ̀. | Tsiku ndi tsiku akuluakulu aŵiri aja ankamuwona akuyenda m'dimbamo, ndipo ankalakalaka kuchita naye zadama. | ||||||||||||||
| 13:9 | They suppressed their consciences and turned away their eyes from looking to Heaven or remembering their duty to administer justice. | Ⲁⲩⲫⲱⲛϩ ⲙ̀ⲡⲟⲩϩⲏⲧ ⲟⲩⲟϩ ⲙⲁϣⲑⲁⲙ ⲛ̀ⲛⲟⲩⲃⲁⲗ ⲉ̀ϣ̀ⲧⲉⲙϫⲟⲩϣⲧ ⲉ̀ⲡ̀ϣⲱⲓ ⲉ̀ⲧ̀ⲫⲉ ⲟⲩⲇⲉ ⲉ̀ϣ̀ⲧⲉⲙⲉⲣⲫ̀ⲙⲉⲩⲓ̀ ⲉ̀ϩⲁⲛϩⲁⲡ ⲛ̀ⲑ̀ⲙⲏⲓ. | Maganizo ao adasanduka opotoka kotero kuti adaleka kupemphera kwa Mulungu, osakumbukiranso kuweruza kolungama. | ||||||||||||||
| 13:10 | Both were overwhelmed with passion for her, but they did not tell each other of their distress, | Ⲟⲩⲟϩ ⲛ̀ⲑⲱⲟⲩ ⲙ̀ⲡ̀ⲃ̅ ⲛⲁⲣⲉ ⲡⲟⲩϩⲏⲧ ⲙⲉⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲣⲟⲥ ⲡⲉ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲩⲟⲩⲱⲛϩ ⲙ̀ⲡⲟⲩⲙ̀ⲕⲁϩ ⲁⲛ ⲡⲉ ⲉ̀ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ. | Onse aŵiri ankamukhumbira kwambiri mkaziyo, koma sankauzana za maganizo aowo. | ||||||||||||||
| 13:11 | for they were ashamed to disclose their lustful desire to seduce her. | Ϫⲉ ⲟⲩⲏⲓ ⲛⲁⲩϣⲓⲡⲓ ⲡⲉ ⲉ̀ⲟⲩⲱⲛϩ ⲛ̀ⲧⲟⲩⲉ̀ⲡⲓⲑⲩⲙⲓⲁ̀ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲉⲑⲃⲉ ϫⲉ ⲛⲁⲩⲟⲩⲱϣ ⲉ̀ϣⲱⲡⲓ ⲛⲉⲙⲁⲥ ⲙ̀ⲡ̀ⲃ̅ ⲡⲉ. | Zidaatero chifukwa ankachita manyazi kunena kuti ankafuna kugona naye. | ||||||||||||||
| 13:12 | Day after day they watched eagerly to see her. | Ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲩϯϩ̀ⲑⲏⲟⲩ ⲙ̀ⲙⲏⲛⲓ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲙⲉⲓ ⲉⲩⲟⲩⲱϣ ⲉ̀ⲛⲁⲩ ⲉ̀ⲣⲟⲥ ⲡⲉϫⲱⲟⲩ ⲇⲉ ⲛ̀ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ. | Tsiku ndi tsiku ankafunafuna mpata woti amuwonere. | ||||||||||||||
| 13:13 | One day they said to each other, Let us go home, for it is time for lunch. So they both left and parted from each other. | ϫⲉ ⲙⲁⲣⲉⲛϣⲉⲛⲁⲛ ⲉ̀ⲡⲉⲛⲏⲓ ϫⲉ ⲟⲩⲏⲓ ⲫ̀ⲛⲁⲩ ⲛ̀ⲟⲩⲱⲙ ⲡⲟⲩⲟϩ ⲉⲧⲁⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲁⲩⲫⲱⲣϫ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲛ̀ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ. | Ndiye tsiku lina adauzana kuti, “Tiyeni tipite kunyumba, yakwana nthaŵi yakudya chakudya chamasana.” | ||||||||||||||
| 13:14 | But turning back, they met again; and when each pressed the other for the reason, they confessed their lust. Then together they arranged for a time when they could find her alone. | Ⲉⲧⲁⲩⲧⲁⲥⲑⲟ ⲁⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲟⲩⲙⲁ ⲉⲩⲥⲟⲡ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲩϣⲓⲛⲓ ⲛ̀ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ ⲛ̀ϯⲉ̀ⲧⲓⲁ̀ ⲟⲩⲟϩ ⲁⲩⲟⲩⲱⲛϩ ⲛ̀ⲧⲟⲩⲉ̀ⲡⲓⲑⲩⲙⲓⲁ̀ ⲛ̀ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ ⲧⲟⲧⲉ ⲁⲩϯⲛⲉⲓ ⲉⲩⲥⲟⲡ ⲉⲑⲃⲉ ⲟⲩⲥⲏⲟⲩ ⲉⲩⲛⲁϫⲉⲙⲥ ⲙ̀ⲙⲁⲩⲁⲧⲥ. | Adasiyanadi, nachita ngati aliyense akupita kwao. Koma posachedwa aliyense adabwerera kudzafuna Suzana, ndiye gululu akumana. Pofunsana bwino zolinga zao, aliyense adaulula mosabisa kuti ankafuna Suzana. Choncho adangopangana nthaŵi yoti adzampeze ali yekha. | ||||||||||||||
| 13:15 | Once, while they were watching for an opportune day, she went in as before with only two maids, and wished to bathe in the garden, for it was a hot day. | Ⲁⲥϣⲱⲡⲓ ⲉ̀ⲡ̀ϫⲓⲛⲧⲟⲩϯ ⲛ̀ϩ̀ⲑⲏⲟⲩ ⲉ̀ⲟⲩⲉ̀ϩⲟⲟⲩ ⲉϥϩⲟⲩⲣⲱⲟⲩ ⲁⲥⲓ̀ ⲉ̀ϧⲟⲩⲛ ⲛ̀ϫⲉ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲙ̀ⲫ̀ⲣⲏϯ ⲛ̀ⲥⲁϥ ⲛⲉⲙ ⲅ̅ ⲙ̀ⲫⲟⲟⲩ ⲉ̀ϧⲟⲩⲛ ⲉ̀ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲛⲉⲙ ⲁ̀ⲗⲟⲩ ⲥ̀ⲛⲟⲩϯ ⲛ̀ⲧⲁⲥ ⲙ̀ⲙⲁⲩⲁⲧⲟⲩ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲥⲉⲣⲉ̀ⲡⲓⲑⲩⲙⲓⲛ ⲉ̀ϫⲱⲕⲉⲙ ϧⲉⲛ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ϫⲉ ⲟⲩⲏⲓ ⲛⲉ ⲡ̀ⲕⲁⲩⲙⲁ ⲡⲉ. | M'mene iwo ankadikira tsiku labwino, Suzana adapita tsiku lina ku dimba ndi adzakazi aŵiri okha, monga ankachitira nthaŵi zonse. Kunkatentha, ndipo adafuna kukasamba kumeneko. | ||||||||||||||
| 13:16 | No one was there except the two elders, who had hidden themselves and were watching her. | Ⲟⲩⲟϩ ⲛⲉ ⲙ̀ⲙⲟⲛ ϩ̀ⲗⲓ ⲙ̀ⲙⲁⲩ ⲡⲉ ⲉⲃⲏⲗ ⲉ̀ⲡⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥⲃ̅ ⲉⲩⲭⲏⲡ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲁⲩϯⲛⲓⲁ̀ⲧⲟⲩ ⲛⲁⲥ ⲡⲉ. | Munalibenso wina aliyense m'dimbamo, kupatula akuluakulu aŵiri aja, amene adaabisala nkumamsuzumira Suzanayo. | ||||||||||||||
| 13:17 | She said to her maids, Bring me olive oil and ointments, and shut the garden doors so that I can bathe. | Ⲡⲉϫⲁⲥ ⲛ̀ⲛⲉⲥⲁ̀ⲗⲱⲟⲩⲓ̀ ϫⲉ ⲁ̀ⲛⲟⲩⲓ̀ ⲛⲏⲓ ⲛ̀ⲟⲩⲛⲉϩ ⲛⲉⲙ ⲟⲩⲥⲙⲏⲙⲁ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲓⲣⲱⲟⲩ ⲛ̀ⲧⲉ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲙⲁϣⲑⲁⲙ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ ϩⲓⲛⲁ ⲛ̀ⲧⲁϫⲱⲕⲉⲙ. | Iye adatuma adzakazi ake aŵiri aja kuti, “Takanditengerani mafuta ndi zonunkhira, tsono mutsekeko zitseko m'dimba muno kuti ndisambe.” | ||||||||||||||
| 13:18 | They did as she told them: they shut the doors of the garden and went out by the side doors to bring what they had been commanded; they did not see the elders, because they were hiding. | Ⲟⲩⲟϩ ⲁⲩⲓ̀ⲣⲓ ⲕⲁⲧⲁ ⲫ̀ⲣⲏϯ ⲉⲧⲁⲥϫⲟⲥ ⲁⲩⲙⲁϣⲑⲁⲙ ⲛ̀ⲛⲓⲣⲱⲟⲩ ⲛ̀ⲧⲉ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲁⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ϧⲉⲛ ⲡⲓⲣⲟ ⲥⲁⲧⲟⲧⲟⲩ ⲉ̀ⲓ̀ⲛⲓ ⲛ̀ⲛⲏⲉⲧⲁⲥⲟⲩⲁϩⲥⲁϩⲛⲓ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ ⲛⲱⲟⲩ ⲟⲩⲟϩ ⲙ̀ⲡⲟⲩⲛⲁⲩ ⲉ̀ⲡⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥ ⲃ̅ ϫⲉ ⲟⲩⲏⲓ ⲛⲁⲩⲭⲏⲡ ⲡⲉ. | Adzakaziwo adachitadi zimene adaaŵauzazo. Adatseka zitseko natulukira pa khomo lina lakumbali kukatenga zinthu zimene adaaŵatumazo. Sadaŵaone akuluakulu aja, chifukwa adaabisala. | ||||||||||||||
| 13:19 | When the maids had gone out, the two elders got up and ran to her. | Ⲁⲥϣⲱⲡⲓ ⲉⲧⲁⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲓⲁ̀ⲗⲱⲟⲩⲓ̀ ⲁⲩⲧⲱⲟⲩⲛⲟⲩ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥⲃ̅ ⲁⲩϭⲟϫⲓ ϩⲁⲣⲟⲥ ⲟⲩⲟϩ ⲡⲉϫⲱⲟⲩ ⲛⲁⲥ. | Adzakazi aja atangochoka, akuluakulu aja adaimirira, nathamangira Suzana. | ||||||||||||||
| 13:20 | They said, Look, the garden doors are shut, and no one can see us. We are burning with desire for you; so give your consent, and lie with us. | Ϫⲉ ϩⲏⲡⲡⲉ ⲓⲥ ⲛⲓⲣⲱⲟⲩ ⲛ̀ⲧⲉ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲥⲉϣⲟⲧⲉⲙ ⲟⲩⲟϩ ⲙ̀ⲙⲟⲛ ϩ̀ⲗⲓ ⲛⲁⲩ ⲉ̀ⲣⲟⲛ ⲧⲉⲛ ⲉ̀ϧ̀ⲣⲏⲓ ϧⲉⲛ ⲧⲉⲛⲉ̀ⲡⲓⲑⲩⲙⲓⲁ̀ ϯⲛⲟⲩ ϫⲉ ⲙⲁⲧⲟϯ ⲛⲁⲛ ϣⲱⲡⲓ ⲛⲉⲙⲁⲛ. | Adamuuza kuti, “Mai, onani zitseko za m'dimba muno nzotseka, palibe amene angatiwone. Pepani, kutereku ife tikukufunani, ndiye mutivomere basi. | ||||||||||||||
| 13:21 | If you refuse, we will testify against you that a young man was with you, and this was why you sent your maids away. | Ⲙ̀ⲙⲟⲛ ⲧⲉⲛⲛⲁⲉⲣⲙⲉⲑⲣⲉ ϧⲁⲣⲟ ϫⲉ ⲛⲁϥϣⲟⲡ ⲛⲉⲙⲉ ⲛ̀ϫⲉ ⲟⲩϧⲉⲗϣⲓⲣⲓ ⲉⲑⲃⲉ ⲫⲁⲓ ⲁⲣⲉⲟⲩⲱⲣⲡ ⲛ̀ⲛⲓⲁ̀ⲗⲱⲟⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲃⲟⲗϩⲁⲣⲟ. | Tangoyesani kukana, ife tikuzengani mlandu woti munali ndi mnyamata, nchifukwa chake mudapirikitsa adzakazi anu.” | ||||||||||||||
| 13:22 | Susanna groaned and said, I am completely trapped. For if I do this, it will mean death for me; if I do not, I cannot escape your hands. | Ⲁⲥϥⲓⲁ̀ϩⲟⲙ ⲛ̀ϫⲉ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲟⲩⲟϩ ⲡⲉϫⲁⲥ ϫⲉ ϯϩⲉϫϩⲱϫ ⲙ̀ⲫⲟⲟⲩ ⲥⲁⲥⲁ ⲛⲓⲃⲉⲛ ⲉϣⲱⲡ ⲁⲓϣⲁⲛⲉⲣ ⲫⲁⲓ ⲟⲩⲙⲟⲩ ⲛⲏⲓ ⲡⲉ ⲉϣⲱⲡ ⲁⲓϣ̀ⲧⲉⲙⲁⲓϥ ⲟⲛ ϯⲛⲁϣ̀ⲫⲱⲧ ⲁⲛ ⲉ̀ⲃⲟⲗϧⲉⲛ ⲛⲉⲧⲉⲛϫⲓϫ. | Suzana adatsitsa moyo, nati, “Nanga ine nditani? Ndikavomera zimenezi, ndiye kuti kwanga nkukaphedwa. Ndikakana, sindipulumuka m'manja mwanu. | ||||||||||||||
| 13:23 | I choose not to do it; I will fall into your hands, rather than sin in the sight of the Lord. | Ⲁⲗⲗⲁ ⲛⲁⲛⲉⲥ ⲛⲏⲓ ⲉ̀ϣ̀ⲧⲉⲙⲁⲓϥ ⲉ̀ⲣⲁⲟⲩⲱ̀ ϧⲉⲛ ⲛⲉⲧⲉⲛϫⲓϫ ⲉϩⲟⲧⲉ ⲉⲣⲛⲟⲃⲓ ⲙ̀ⲡⲉⲙ̀ⲑⲟ ⲙ̀Ⲫϯ ⲛ̀ⲧⲉ ⲧ̀ⲫⲉ. | Koma ai, ine ndikuti toto. Ndi bwino kuti mundiphe, kupambana kuti ndichimwire Ambuye.” | ||||||||||||||
| 13:24 | Then Susanna cried out with a loud voice, and the two elders shouted against her. | Ⲁⲥⲱϣ ⲉ̀ⲡ̀ϣⲱⲓ ⲛ̀ϫⲉ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲛⲓϣϯ ⲛ̀ⲥ̀ⲙⲏ ⲁⲩⲱϣ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ϩⲱⲟⲩ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥⲃ̅ ⲙ̀ⲡⲉⲥⲙ̀ⲑⲟ. | Motero Suzana adafuula kwambiri, akuluakulu aja nawonso adayamba kufuula. | ||||||||||||||
| 13:25 | And one of them ran and opened the garden doors. | Ⲟⲩⲟϩ ⲉⲧⲁϥϭⲟϫⲓ ⲛ̀ϫⲉ ⲟⲩⲁⲓ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ ⲁϥⲟⲩⲱⲛ ⲛ̀ⲛⲓⲣⲱⲟⲩ ⲛ̀ⲧⲉ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ. | Mmodzi mwa iwo adakatsekula chitseko cha m'dimba. | ||||||||||||||
| 13:26 | When the people in the house heard the shouting in the garden, they rushed in at the side door to see what had happened to her. | Ϩⲱⲥ ⲇⲉ ⲉⲧⲁⲩⲥⲱⲧⲉⲙ ⲉ̀ⲡⲓϧ̀ⲣⲱⲟⲩ ϧⲉⲛ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲁ ⲡⲉⲥⲏⲓ ⲁⲩϣⲉⲛⲱⲟⲩ ⲥⲁⲧⲟⲧⲟⲩ ⲉ̀ⲛⲁⲩ ϫⲉ ⲟⲩ ⲡⲉ ⲉⲧⲁϥϣⲱⲡⲓ ⲙ̀ⲙⲟⲥ. | Antchito akunyumba atamva kufuula ku dimba, adathamangira khomo lakumbali, kuti akaone chimene chamchitikira Suzana. | ||||||||||||||
| 13:27 | And when the elders told their story, the servants felt very much ashamed, for nothing like this had ever been said about Susanna. | Ⲁⲥϣⲱⲡⲓ ⲇⲉ ⲉⲧⲁ ⲛⲓⲡⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥ ϫⲉ ⲛⲟⲩⲥⲁϫⲓ ⲁⲩϣ̀ⲫⲓⲧ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲓⲉ̀ⲃⲓⲁⲓⲕ ⲉⲙⲁϣⲱ ϫⲉ ⲙ̀ⲡⲟⲩϫⲉⲙ ⲟⲩⲥⲁϫⲓ ⲙ̀ⲡⲁⲓⲣⲏϯ ⲉ̀ⲛⲉϩ ϧⲁ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ. | Akuluakulu aja atafotokoza nkhani yao, antchito aja adagwidwa ndi manyazi, chifukwa chikhalire sadamumverepo zotere Suzana. | ||||||||||||||
| 13:28 | The next day, when the people gathered at the house of her husband Joakim, the two elders came, full of their wicked plot to have Susanna put to death. In the presence of the people they said, | Ⲁⲥϣⲱⲡⲓ ⲇⲉ ⲉ̀ⲡⲉϥⲣⲁⲥϯ ⲉⲧⲁϥⲓ̀ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ϩⲁ Ⲓⲱⲁⲕⲓⲙ ⲡⲉⲥϩⲁⲓ ⲁⲩⲓ̀ ϩⲱⲟⲩ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥⲃ̅ ⲉⲩⲙⲉϩ ⲙ̀ⲙⲉⲩⲓ̀ ⲛ̀ⲁ̀ⲛⲟⲙⲓⲁ̀ ϧⲁ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲉ̀ⲡ̀ϫⲓⲛϧⲟⲑⲃⲉⲥ. | M'maŵa mwake, pamene anthu adaasonkhana kunyumba kwa mwamuna wake Yowakimu, akuluakulu aŵiri aja adafika, atatsimikiza zofuna kulipsira, kuti Suzana aphedwe. | ||||||||||||||
| 13:29 | Send for Susanna daughter of Hilkiah, the wife of Joakim. | Ⲟⲩⲟϩ ⲡⲉϫⲱⲟⲩ ⲙ̀ⲡⲉⲙ̀ⲑⲟ ⲙ̀ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ϫⲉ ⲟⲩⲱⲣⲡ ⲛ̀ⲥⲁ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲧ̀ϣⲉⲣⲓ ⲛ̀Ⲭⲁⲗⲕⲓⲁⲥ ⲧ̀ⲥ̀ϩⲓⲙⲓ ⲛ̀Ⲓⲱⲁⲕⲓⲙ ⲛ̀ⲑⲱⲟⲩ ⲇⲉ ⲁⲩⲟⲩⲱⲣⲡ. | Pamaso pa anthuwo adati, “Kaitaneni Suzana mwana wa Hilikiya, mkazi wa Yowakimu.” | ||||||||||||||
| 13:30 | So they sent for her. And she came with her parents, her children, and all her relatives. | Ⲁⲥⲓ̀ ⲛ̀ϫⲉ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲛⲉⲙ ⲛⲉⲥⲓⲟϯ ⲛⲉⲙ ⲛⲉⲥϣⲏⲣⲓ ⲛⲉⲙ ⲛⲉⲥⲥⲩⲅⲅⲉⲛⲏⲥ ⲧⲏⲣⲟⲩ. | Adapita kukamuitana, iye nkubwera pamodzi ndi makolo ake, ana ake ndi anansi ake onse. | ||||||||||||||
| 13:31 | Now Susanna was a woman of great refinement and beautiful in appearance. | Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲇⲉ ⲛⲉ ⲟⲩⲥⲁⲓⲏ ⲧⲉ ϧⲉⲛ ⲡⲉⲥⲥ̀ⲙⲟⲧ ⲟⲩⲟϩ ⲉⲛⲁⲛⲉⲥ ⲉⲙⲁϣⲱ ⲧⲉ. | Suzanatu anali wa nkhope yochititsa chidwi ndi yokongola. | ||||||||||||||
| 13:32 | As she was veiled, the scoundrels ordered her to be unveiled, so that they might feast their eyes on her beauty. | Ⲛⲓⲡⲁⲣⲁⲛⲟⲙⲟⲥ ⲇⲉ ⲁⲩⲉⲣⲕⲉⲗⲉⲩⲓⲛ ⲉ̀ⲟⲩⲃⲁϣ ϫⲱⲥ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲛⲁⲣⲉ ϫⲱⲥ ⲅⲁⲣ ϩⲟⲃⲥ ⲡⲉ ϩⲟⲡⲱⲥ ⲛ̀ⲧⲟⲩⲥⲓ ⲙ̀ⲡⲉⲥⲥⲁⲓ. | Pamene ankafika pa bwalo, anali atavala nsalu yochinga kumaso. Tsono anthu oipa aja adalamula kuti amuchotse nsaluyo kumaso, kuti amuwone bwino kukongola kwake. | ||||||||||||||
| 13:33 | Those who were with her and all who saw her were weeping. | Ⲛⲁⲩⲣⲓⲙⲓ ⲧⲏⲣⲟⲩ ⲡⲉ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲏⲉⲑⲛⲁⲩ ⲉ̀ⲣⲟⲥ ⲛⲉⲙ ⲛⲏⲉⲧⲏⲡ ⲉ̀ⲣⲟⲥ ⲧⲏⲣⲟⲩ. | Am'banja mwake pamodzi ndi anthu onse amene adamuwona, adayamba kulira. | ||||||||||||||
| 13:34 | Then the two elders stood up before the people and laid their hands on her head. | Ⲁⲩⲧⲱⲟⲩⲛⲟⲩ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥ ϧⲉⲛ ⲑ̀ⲙⲏϯ ⲙ̀ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ⲁⲩⲭⲏ ⲛ̀ⲛⲟⲩϫⲓϫ ⲉ̀ϩ̀ⲣⲏⲓ ⲉ̀ϫⲉⲛ ⲧⲉⲥⲁ̀ⲫⲉ. | Akuluakulu aja adaimirira pamaso pa anthu aja, nasanjika manja pamutu pa Suzana. | ||||||||||||||
| 13:35 | Through her tears she looked up toward Heaven, for her heart trusted in the Lord. | Ⲛ̀ⲑⲟⲥ ⲇⲉ ⲁⲥⲣⲓⲙⲓ ⲁⲥϫⲟⲩϣⲧ ⲉ̀ϩ̀ⲣⲏⲒ ⲉ̀ⲧ̀ⲫⲉ ϫⲉ ⲟⲩⲏⲓ ⲡⲉⲥϩⲏⲧ ⲟⲩⲉϩ ⲉ̀Ⲫϯ ⲡⲉ. | Iye adayang'ana kumwamba akulira, chifukwa ankakhulupirira Mulungu. | ||||||||||||||
| 13:36 | The elders said, While we were walking in the garden alone, this woman came in with two maids, shut the garden doors, and dismissed the maids. | Ⲡⲉϫⲱⲟⲩ ⲇⲉ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥ ϫⲉ ⲉ̀ⲛⲁⲛⲙⲟϣⲓ ⲙ̀ⲙⲁⲩⲁⲧⲉⲛ ⲡⲉ ϧⲉⲛ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲁⲥⲓ̀ ⲉ̀ϧⲟⲩⲛ ⲛ̀ϫⲉ ⲑⲁⲓ ⲛⲉⲙ ⲃⲱⲕⲓ ⲥ̀ⲛⲟⲩϯ ⲁⲥⲟⲩⲱⲣⲡ ⲛ̀ⲛⲓⲃⲱⲕⲓ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲟⲩⲟϩ ⲁⲩⲙⲁϣⲑⲁⲙ ⲛ̀ⲛⲓⲣⲱⲟⲩ ⲛ̀ⲧⲉ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ. | Akuluakuluwo adati, “Ife tinkangodziyendera tokha m'dimbamu. Tidangoona mkazi uyu akufika ndi adzakazi ake aŵiri. Adatseka zitseko za m'dimba, adzakazi aja nkuŵabweza kunyumba. | ||||||||||||||
| 13:37 | Then a young man, who was hiding there, came to her and lay with her. | Ⲁϥⲓ̀ ϩⲁⲣⲟⲥ ⲛ̀ϫⲉ ⲟⲩϧⲉⲗϣⲓⲣⲓ ⲉϥⲭⲏⲡ ϧⲉⲛ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲁϥⲛ̀ⲕⲟⲧ ⲛⲉⲙⲁⲥ. | Tsono mnyamata wina amene adaabisala, adapita kwa iye, nkugona naye. | ||||||||||||||
| 13:38 | We were in a corner of the garden, and when we saw this wickedness we ran to them. | Ⲁⲛⲟⲛ ⲇⲉ ⲉⲛⲭⲏⲡ ϧⲉⲛ ϯⲉⲗⲕⲥ ⲛ̀ⲧⲉ ⲡⲓⲡⲁⲣⲁⲇⲓⲥⲟⲥ ⲉⲧⲁⲛⲛⲁⲩ ⲉ̀ϯⲁ̀ⲛⲟⲙⲓⲁ̀ ⲁⲛϭⲟϫⲓ ⲉ̀ϩ̀ⲣⲏⲓ ⲉ̀ϫⲱⲟⲩ ⲁⲛⲛⲁⲩ ⲉ̀ⲣⲱⲟⲩ ⲉⲩϣⲟⲡ ⲛⲉⲙ ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ. | Ife nkuti tili ku mapeto a dimba. Tsono poona zoipa zinkachitikazo, tidathamangira komweko. | ||||||||||||||
| 13:39 | Although we saw them embracing, we could not hold the man, because he was stronger than we, and he opened the doors and got away. | Ⲫⲏ ⲙⲉⲛ ⲙ̀ⲡⲉⲛϣ̀ϫⲉⲙϫⲟⲙ ⲉ̀ⲁ̀ⲙⲁϩⲓ ⲙ̀ⲙⲟϥ ⲉⲑⲃⲉ ϫⲉ ⲛⲁϥϫⲟⲣ ⲉϩⲟⲧⲉⲣⲟⲛ ⲟⲩⲟϩ ⲁϥⲟⲩⲱⲛ ⲛ̀ⲛⲓⲣⲱⲟⲩ ⲁϥⲫⲱⲧ ⲁϥϣⲉⲛⲁϥ. | Ngakhale tidaŵaona atakumbatirana, sitidathe kumugwira mwamunayo. Anali wamphamvu kwambiri, choncho adatsekula chitseko nkuthaŵa. | ||||||||||||||
| 13:40 | We did, however, seize this woman and asked who the young man was, | Ⲑⲁⲓ ⲇⲉ ⲁⲛⲁ̀ⲙⲟⲛⲓ ⲙ̀ⲙⲟⲥ ⲁⲛϣⲉⲛⲥ ϫⲉ ⲛⲓⲙ ⲡⲉ ⲡⲁⲓϧⲉⲗϣⲓⲣⲓ ⲟⲩⲟϩ ⲙ̀ⲡⲉⲥⲟⲩⲱϣ ⲉ̀ⲧⲁⲙⲟⲛ ⲛⲁⲓ ⲅⲁⲣ ⲧⲉⲛⲉⲣⲙⲉⲑⲣⲉ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ ⲁ̀ⲛⲟⲛ. | Tidangogwirako mkaziyu, nkumufunsa za mnyamatayo, koma adakana kutiwuza chilichonse. Tikulumbira kuti umboni wathuwu ngwoona.” | ||||||||||||||
| 13:41 | but she would not tell us. These things we testify. Because they were elders of the people and judges, the assembly believed them and condemned her to death. | Ⲟⲩⲟϩ ⲁⲥⲧⲉⲛϩⲟⲩⲧⲟⲩ ⲛ̀ϫⲉ ϯⲥⲩⲛⲁⲅⲱⲅⲏ ⲧⲏⲣⲥ ϩⲱⲥ ϩⲁⲛⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥ ⲛⲉ ⲟⲩⲟϩ ϩⲁⲛⲕ̀ⲣⲓⲧⲏⲥ ⲛ̀ⲧⲉ ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ⲁⲩϯϩⲁⲡ ⲉ̀ⲣⲟⲥ ⲉⲑⲣⲉⲥⲙⲟⲩ. | Poti akuluakulu aja anali oyang'anira ndi oweruza anthu, onse amene adaadzasonkhana pamenepo adaŵakhulupirira, navomereza kuti Suzana aphedwe. | ||||||||||||||
| 13:42 | Then Susanna cried out with a loud voice, and said, O eternal God, you know what is secret and are aware of all things before they come to be; | Ⲁⲥⲱϣ ⲉ̀ⲡ̀ϣⲱⲓ ⲛ̀ϫⲉ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲛⲓϣϯ ⲛ̀ⲥ̀ⲙⲏ ⲟⲩⲟϩ ⲡⲉϫⲁⲥ ϫⲉ Ⲫϯ ⲡⲓϣⲁⲉ̀ⲛⲉϩ ⲫⲏⲉⲧⲥⲱⲟⲩⲛ ⲛ̀ⲛⲏⲉⲧϩⲏⲡ ⲫⲏⲉⲧⲥⲱⲟⲩⲛ ⲛ̀ϩⲱⲃ ⲛⲓⲃⲉⲛ ⲙ̀ⲡⲁⲧⲟⲩϣⲱⲡⲓ. | Apo Suzana adanena mokweza mau kuti, “Inu Mulungu wamuyaya, mumadziŵa zinsinsi zonse, mumadziŵiratu zinthu zonse zisanachitike nkomwe. | ||||||||||||||
| 13:43 | you know that these men have given false evidence against me. And now I am to die, though I have done none of the wicked things that they have charged against me! | Ⲛ̀ⲑⲟⲕ ⲉⲧⲥⲱⲟⲩⲛ ⲱ̀ Ⲡϭ̅ⲥ̅ ϫⲉ ⲉⲣⲉ ⲛⲁⲓ ⲉⲣⲙⲉⲑⲣⲉ ⲛ̀ⲛⲟⲩϫ ϧⲁⲣⲟⲓ ϩⲏⲡⲡⲉ ϯⲛⲁⲙⲟⲩ ⲙ̀ⲡⲓⲉⲣ ϩ̀ⲗⲓ ⲛ̀ⲛⲟⲃⲓ ⲛ̀ⲛⲏⲉⲧⲉ ⲛⲁⲓ ⲙⲉⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲣⲟⲓ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ. | Mukudziŵa kuti anthuŵa akundinyengezera. Tsopano ndilikufa, komabe ine sindidachite konse zimene andinenezazi.” | ||||||||||||||
| 13:44 | The Lord heard her cry. | Ⲁϥⲥⲱⲧⲉⲙ ⲛ̀ϫⲉ Ⲡϭ̅ⲥ̅ ⲉ̀ⲧⲉⲥⲥ̀ⲙⲏ. | Ambuye adamva pemphero lakelo. | ||||||||||||||
| 13:45 | Just as she was being led off to execution, God stirred up the holy spirit of a young lad named Daniel, | Ⲉⲩⲱ̀ⲗⲓ ⲙ̀ⲙⲟⲥ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲉ̀ⲧⲁⲕⲟⲥ ⲁ Ⲫϯ ⲧⲟⲩⲛⲟⲥ ⲟⲩⲡ̅ⲛ̅ⲁ̅ ⲉϥⲟⲩⲁⲃ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲁ̀ⲗⲟⲩ ⲙ̀ⲃⲉⲣⲓ ⲉ̀ⲡⲉϥⲣⲁⲛ ⲡⲉ Ⲇⲁⲛⲓⲏⲗ. | Pamene anthu ankapita naye kukamupha, Mulungu adautsa nzeru mwa mnyamata wina dzina lake Daniele. | ||||||||||||||
| 13:46 | and he shouted with a loud voice, I want no part in shedding this woman's blood! | Ⲁϥⲱϣ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲛⲓϣϯ ⲛ̀ϧ̀ⲣⲱⲟⲩ ϫⲉ ϯⲟⲩⲁⲃ ⲁ̀ⲛⲟⲕ ⲉ̀ⲃⲟⲗϩⲁ ⲡ̀ⲥ̀ⲛⲟϥ ⲛ̀ⲧⲉ ⲧⲁⲓⲥ̀ϩⲓⲙⲓ. | Iyeyo mokweza mau adati, “Ine musandiŵerengereko pa imfa ya mai ameneyu.” | ||||||||||||||
| 13:47 | All the people turned to him and asked, What is this you are saying? | Ⲁϥⲧⲁⲥⲑⲟ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ⲧⲏⲣϥ ϩⲁⲣⲟϥ ⲟⲩⲟϩ ⲡⲉϫⲱⲟⲩ ϫⲉ ⲡⲁⲓⲥⲁϫⲓ ⲟⲩ ⲡⲉ ⲉⲧⲁⲕϫⲟϥ ⲛ̀ⲑⲟⲕ. | Anthu onse adamcheukira, namufunsa kuti, “Iwe ukuti chiyani?” | ||||||||||||||
| 13:48 | Taking his stand among them he said, Are you such fools, O Israelites, as to condemn a daughter of Israel without examination and without learning the facts? | Ⲛ̀ⲑⲟϥ ⲇⲉ ⲁϥⲟ̀ϩⲓ ⲉ̀ⲣⲁⲧϥ ϧⲉⲛ ⲧⲟⲩⲙⲏϯ ⲡⲉϫⲁϥ ϫⲉ ⲡⲁⲓⲣⲏϯ ⲛ̀ⲑⲱⲧⲉⲛ ϩⲁⲛⲥⲟϫ ϧⲁ ⲛⲉⲛϣⲏⲣⲓ ⲙ̀Ⲡⲓ̅ⲥ̅ⲗ̅ ϫⲉ ⲙ̀ⲡⲉⲧⲉⲛϧⲟⲧⲱⲉⲧ ⲟⲩⲇⲉ ϯⲙⲉⲧⲥⲁⲃⲉ ⲙ̀ⲡⲉⲧⲉⲛⲥⲟⲩⲱⲛⲥ ⲁⲣⲉⲧⲉⲛϩⲓ ⲧ̀ϣⲉⲣⲓ ⲙ̀Ⲡⲓ̅ⲥ̅ⲗ̅ ⲉ̀ⲡ̀ϩⲁⲡ. | Daniele adaimirira nati, “Inu Aisraele, kodi mungapuse chotere? Inu mungagamule kuti mai Wachiisraele aphedwe, musanafufuze nkhani ndi kupeza chenicheni chimene adalakwa? | ||||||||||||||
| 13:49 | Return to court, for these men have given false evidence against her. | Ⲁⲗⲗⲁ ⲙⲁⲧⲁⲥⲑⲟ ⲉ̀ⲡⲓⲙⲁⲛ̀ϯϩⲁⲡ ⲉⲧⲁ ⲛⲁⲓ ⲅⲁⲣ ⲉⲣⲙⲉⲑⲣⲉ ⲛ̀ⲛⲟⲩϫ ϧⲁⲣⲟⲥ. | Uyambeninso mlanduwu, umboni umene apereka anthu aŵa, kuneneza maiyu, ngwonama.” | ||||||||||||||
| 13:50 | So all the people hurried back. And the rest of the elders said to him, Come, sit among us and inform us, for God has given you the standing of an elder. | Ⲁϥⲧⲁⲥⲑⲟ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲓⲏⲥ ⲡⲉϫⲱⲟⲩ ⲛⲁϥ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥ ϫⲉ ⲁ̀ⲙⲟⲩ ϩⲉⲙⲥⲓ ϧⲉⲛ ⲧⲉⲛⲙⲏϯ ⲟⲩⲟϩ ⲙⲁⲧⲁⲙⲟⲛ ϫⲉ ⲛ̀ⲑⲟⲕ ⲁ Ⲫϯ ϯ ⲛⲁⲕ ⲙ̀ⲡⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲏⲣⲓⲟⲛ. | Tsono anthu adabwerera ku bwalo lamilandu, ndipo akuluakulu ena adauza Daniele kuti, “Dzakhale nafe, udzatiwuze zimene uli nazo kukhosi, chifukwa Mulungu wakupatsa nzeru ngati za akulu.” | ||||||||||||||
| 13:51 | Daniel said to them, Separate them far from each other, and I will examine them. | Ⲟⲩⲟϩ ⲡⲉϫⲉ Ⲇⲁⲛⲓⲏⲗ ϫⲉ ⲫⲟⲣϫⲟⲩ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲉ̀ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ ϩⲓⲛⲁ ⲛ̀ⲧⲁⲉⲣⲁ̀ⲛⲁⲕⲣⲓⲛⲓⲛ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ. | Daniele adaŵauza kuti, “Muŵalekanitse anthu oweruzaŵa, akhalirane kutali, kenaka ndiŵafunsitsa bwino.” | ||||||||||||||
| 13:52 | When they were separated from each other, he summoned one of them and said to him, You old relic of wicked days, your sins have now come home, which you have committed in the past, | Ϩⲱⲥ ⲇⲉ ⲉⲧⲁⲩⲫⲟⲣϫⲟⲩ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲛ̀ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ ⲁϥⲙⲟⲩϯ ⲉ̀ⲟⲩⲁⲓ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲁϥ ϫⲉ ⲫⲏⲉⲧⲁϥⲉⲣⲁ̀ⲡⲁⲥ ϧⲉⲛ ⲛⲉϥⲉ̀ϩⲟⲟⲩ ⲉⲧϩⲱⲟⲩ ϯⲛⲟⲩ ⲁⲩⲒ̀ ⲉ̀ϫⲱⲕ ⲛ̀ϫⲉ ⲛⲉⲕⲛⲟⲃⲓ ⲛⲏⲉ̀ⲛⲁⲕⲓ̀ⲣⲓ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ ⲛ̀ϣⲟⲣⲡ. | Ataŵalekanitsa, Daniele adaitana mmodzi mwa iwo. Adamuuza kuti, “Akulu inu, mudakalambira m'nkhanza, akubwererani machimo anu akale: | ||||||||||||||
| 13:53 | pronouncing unjust judgments, condemning the innocent and acquitting the guilty, though the Lord said, You shall not put an innocent and righteous person to death.' | Ⲉⲕϯϩⲁⲡ ϧⲉⲛ ϩⲁⲛϩⲁⲡ ⲛ̀ⲟ̀ϫⲓ ⲛⲓⲁⲑⲛⲟⲃⲓ ⲉⲕϩⲓⲟⲩⲓ̀ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ ⲉ̀ⲡ̀ϩⲁⲡ ⲟⲩⲟϩ ⲛⲏⲉⲧⲉⲣⲛⲟⲃⲓ ⲉⲕⲭⲱ ⲙ̀ⲙⲱⲟⲩ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲉϥϫⲱ ⲙ̀ⲙⲟⲥ ⲛ̀ϫⲉ Ⲡϭ̅ⲥ̅ ϫⲉ ⲟⲩⲁⲑⲛⲟⲃⲓ ⲛⲉⲙ ⲟⲩⲑ̀ⲙⲏⲓ ⲛ̀ⲛⲉⲕϧⲟⲑⲃⲟⲩ. | Munkagamula milandu mopanda chilungamo: kumalanga osalakwa, nkumamasula olakwa amene. Chonsecho Ambuye adanena kuti, ‘Usaphe munthu wosachimwa ndi wosalakwa.’ | ||||||||||||||
| 13:54 | Now then, if you really saw this woman, tell me this: Under what tree did you see them being intimate with each other? He answered, Under a mastic tree. | Ϯⲛⲟⲩ ⲟⲩⲛ ⲓⲥϫⲉ ⲁⲕⲛⲁⲩ ⲉ̀ⲑⲁⲓ ⲁ̀ϫⲟⲥ ⲛⲏⲓ ϫⲉ ⲉⲧⲁⲕⲧⲁϩⲱⲟⲩ ⲉⲩⲥⲁϫⲓ ⲛⲉⲙ ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ ϧⲁⲧⲉⲛ ⲁϣ ⲛ̀ϣ̀ϣⲏⲛ ⲛ̀ⲑⲟϥ ⲡⲉϫⲁϥ ϫⲉ ϧⲁⲣⲁⲧϥ ⲛ̀ⲟⲩⲥⲭⲓⲛⲟⲛ. | Tsopano ngati mudamuwonadi maiyu akuchimwa ndi mnyamata, mudaŵaona ali patsinde pa mtengo wanji?” Iye adayankha kuti, “Patsinde pa mkuyu.” | ||||||||||||||
| 13:55 | And Daniel said, Very well! This lie has cost you your head, for the angel of God has received the sentence from God and will immediately cut you in two. | Ⲡⲉϫⲉ Ⲇⲁⲛⲓⲏⲗ ϫⲉ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲥⲱⲟⲩⲧⲉⲛ ⲁⲕϫⲉⲙⲉⲑⲛⲟⲩϫ ⲟⲩⲟϩ ⲡⲉⲕⲥⲁⲙⲉⲑⲛⲟⲩϫ ϩⲓϫⲉⲛ ⲧⲉⲕⲁ̀ⲫⲉ ϩⲏⲡⲡⲉ ⲓⲥ ⲡⲓⲁⲅⲅⲉⲗⲟⲥ ⲛ̀ⲧⲉ Ⲡϭ̅ⲥ̅ ⲁϥϭⲓ ⲙ̀ⲡ̀ϣⲓⲛⲓ ⲉ̀ⲃⲟⲗϩⲓⲧⲟⲧϥ ⲙ̀Ⲫϯ ⲉϥⲉ̀ⲫⲟⲣϫⲕ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ϧⲉⲛ ⲧⲉⲕⲙⲏϯ. | Daniele adati, “Ndithudi, bodza lanu lakubwererani. Mngelo wa Mulungu walamulidwa kale kuti akulangeni, adzakudulani pakati.” | ||||||||||||||
| 13:56 | Then, putting him to one side, he ordered them to bring the other. And he said to him, You offspring of Canaan and not of Judah, beauty has beguiled you and lust has perverted your heart. | Ⲟⲩⲟϩ ϩⲟⲧⲉ ⲉⲧⲁⲩⲟⲩⲟⲑⲃⲉϥ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲁϥⲟⲩⲁϩⲥⲁϩⲛⲓ ⲉⲑⲣⲟⲩⲓ̀ⲛⲓ ⲛⲁϥ ⲙ̀ⲡⲓⲭⲉⲧ ⲡⲉϫⲁϥ ⲛⲁϥ ϫⲉ ⲡⲓϫ̀ⲣⲟϫ ⲛ̀Ⲭⲁⲛⲁⲁⲛ ⲟⲩⲟϩ ⲫⲁ Ⲓⲟⲩⲇⲁ ⲁⲛ ⲁ ⲡⲓⲥⲁϫⲓ ⲉⲣϩⲁⲗ ⲙ̀ⲙⲟⲕ ⲟⲩⲟϩ ⲁ ϯⲉ̀ⲡⲓⲑⲩⲙⲓⲁ̀ ⲑⲱⲙ ⲙ̀ⲡⲉⲕϩⲏⲧ. | Atatero adamuuza kuti aime pambali, nalamula anthu aja kuti abwere ndi wina uja. Tsono Daniele adamuuza kuti, “Akulu inu, mukukhala ngati ndinu Mkanani osati Myuda! Kukongola kwa akazi kwakusokonezani, ndipo dama lakusandutsani chitsiru. | ||||||||||||||
| 13:57 | This is how you have been treating the daughters of Israel, and they were intimate with you through fear; but a daughter of Judah would not tolerate your wickedness. | Ⲡⲁⲓⲣⲏϯ ⲛⲁⲣⲉⲧⲉⲛⲣⲁ ⲙ̀ⲙⲟⲥ ⲛ̀ⲛⲉⲛϣⲉⲣⲓ ⲙ̀Ⲡⲓ̅ⲥ̅ⲗ̅ ⲛⲏⲉ̀ⲛⲁⲩⲉⲣϩⲟϯ ⲛⲁⲩⲥⲁϫⲓ ⲛⲉⲙⲱⲧⲉⲛ ⲁⲛ ⲡⲉ ⲁⲗⲗⲁ ⲧ̀ϣⲉⲣⲓ ⲛ̀Ⲓⲟⲩⲇⲁ ⲙ̀ⲡⲉⲥⲉⲣϩⲩⲡⲟⲙⲉⲛⲓⲛ ⲉⲧⲉⲧⲉⲛⲁ̀ⲛⲟⲙⲓⲁ̀. | Ndikudziŵa m'mene mwakhala mukuvutitsira akazi a ku Israele, iwo amangovomera chifukwa cha mantha. Koma mai wa ku Yudayu wakukanikani kuti muchimwe naye. | ||||||||||||||
| 13:58 | Now then, tell me: Under what tree did you catch them being intimate with each other? He answered, Under an evergreen oak. | Ϯⲛⲟⲩ ⲟⲩⲛ ⲁ̀ϫⲟⲥ ⲛⲏⲓ ϫⲉ ⲉⲧⲁⲕⲧⲁϩⲱⲟⲩ ⲉⲩⲥⲁϫⲓ ⲛⲉⲙ ⲛⲟⲩⲉ̀ⲣⲏⲟⲩ ⲛ̀ⲑⲱⲛ ⲛ̀ⲑⲟϥ ⲇⲉ ⲡⲉϫⲁϥ ϫⲉ ϧⲁⲣⲁⲧϥ ⲛ̀ⲟⲩⲡ̀ⲣⲓⲛⲓⲟⲛ. | Tanenani tsono, ndi patsinde pa mtengo wanji mudaŵapezera ali aŵiri?” Iye adayankha kuti, “Patsinde pa mtengo wa thundu.” | ||||||||||||||
| 13:59 | Daniel said to him, Very well! This lie has cost you also your head, for the angel of God is waiting with his sword to split you in two, so as to destroy you both. | Ⲡⲉϫⲉ Ⲇⲁⲛⲓⲏⲗ ⲛⲁϥ ϫⲉ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲥⲱⲟⲩⲧⲉⲛ ϩⲱⲕ ⲟⲛ ⲁⲕϫⲉⲙⲉⲑⲛⲟⲩϫ ⲟⲩⲟϩ ⲡⲉⲕⲥⲁⲙⲉⲑⲛⲟⲩϫ ⲉ̀ϩ̀ⲣⲏⲓ ⲉ̀ϫⲉⲛ ⲧⲉⲕⲁ̀ⲫⲉ ϥ̀ⲟ̀ϩⲓ ⲉ̀ⲣⲁⲧϥ ⲛ̀ϫⲉ ⲡⲓⲁⲅⲅⲉⲗⲟⲥ ⲛ̀ⲧⲉ Ⲫϯ ⲉⲣⲉ ϯⲥⲏϥⲓ ⲭⲏ ⲛ̀ⲧⲟⲧϥ ⲉϥⲟⲩⲁⲥⲕ ϧⲉⲛ ⲧⲉⲕⲙⲏϯ ⲟⲩⲟϩ ⲉϥⲉ̀ⲧⲁⲕⲉ ⲑⲏⲛⲟⲩ ⲙ̀ⲡ̀ⲃ̅. | Daniele adati, “Ndithudi, bodza lanu lakubwererani. Mngelo wa Mulungu akukudikirani ndi lupanga kuti akuchekeni pakati ndi kukuwonongani aŵirinu.” | ||||||||||||||
| 13:60 | Then the whole assembly raised a great shout and blessed God, who saves those who hope in him. | Ⲁⲥⲱϣ ⲉ̀ⲃⲟⲗ ⲛ̀ϫⲉ ϯⲥⲩⲛⲁⲅⲱⲅⲏ ⲧⲏⲣⲥ ϧⲉⲛ ⲟⲩⲛⲓϣϯ ⲛ̀ϧ̀ⲣⲱⲟⲩ ⲟⲩⲟϩ ⲁⲩⲥ̀ⲙⲟⲩ ⲉ̀Ⲫϯ ⲫⲏⲉⲑⲛⲟϩⲉⲙ ⲛ̀ⲛⲏⲉⲧⲉⲣⲉⲣϩⲉⲗⲡⲓⲥ ⲉ̀ⲣⲟϥ. | Pamenepo anthu onse adafuula kwambiri, natamanda Mulungu, Mpulumutsi wa anthu okhulupirira Iye. | ||||||||||||||
| 13:61 | And they took action against the two elders, because out of their own mouths Daniel had convicted them of bearing false witness; they did to them as they had wickedly planned to do to their neighbor. | Ⲟⲩⲟϩ ⲁⲩⲧⲱⲟⲩⲛⲟⲩ ⲉ̀ϩ̀ⲣⲏⲓ ⲉ̀ϫⲉⲛ ⲡⲓⲡ̀ⲣⲉⲥⲃⲩⲧⲉⲣⲟⲥⲃ̅ ϫⲉ ⲁϥⲧⲁϩⲱⲟⲩ ⲛ̀ϫⲉ Ⲇⲁⲛⲓⲏⲗ ⲉ̀ⲃⲟⲗϧⲉⲛ ⲣⲱⲟⲩ ϫⲉ ⲁⲩϫⲉⲙⲉⲑⲛⲟⲩϫ ⲟⲩⲟϩ ⲁⲩⲓ̀ⲣⲓ ⲛⲱⲟⲩ ⲕⲁⲧⲁ ⲫ̀ⲣⲏϯ ⲉ̀ⲛⲁⲩⲙⲉⲩⲓ̀ ⲉ̀ⲉⲣⲡⲉⲧϩⲱⲟⲩ ⲙ̀ⲡⲟⲩϣ̀ⲫⲏⲣ ⲕⲁⲧⲁ ⲫ̀ⲛⲟⲙⲟⲥ ⲙ̀Ⲙⲱⲩ̀ⲥⲏⲥ. | Kenaka adatembenukira oweruza aŵiri aja, amene Daniele adaaŵatsutsa chifukwa chochita umboni wabodza. | ||||||||||||||
| 13:62 | Acting in accordance with the law of Moses, they put them to death. Thus innocent blood was spared that day. | Ⲟⲩⲟϩ ⲁⲩϧⲟⲑⲃⲟⲩ ⲟⲩⲟϩ ⲁϥⲛⲟϩⲉⲙ ⲛ̀ϫⲉ ⲟⲩⲥ̀ⲛⲟϥ ⲛ̀ⲁⲑⲛⲟⲃⲓ ϧⲉⲛ ⲛⲓⲉ̀ϩⲟⲟⲩ ⲉⲧⲉⲙ̀ⲙⲁⲩ. | Adaŵalanga potsata malamulo a Mose, ndi kuŵapha monga momwe iwo ndi kuipa mtima kwao adaafuna kuphera mbale wao. Motero munthu wosalakwa adapulumuka tsiku limenelo. | ||||||||||||||
| 13:63 | Hilkiah and his wife praised God for their daughter Susanna, and so did her husband Joakim and all her relatives, because she was found innocent of a shameful deed. | Ⲭⲉⲗⲕⲓⲁⲥ ⲇⲉ ⲛⲉⲙ ⲧⲉϥⲥ̀ϩⲓⲙⲓ ⲁⲩⲥ̀ⲙⲟⲩ ⲉ̀Ⲫϯ ⲉⲑⲃⲉ ⲧⲟⲩϣⲉⲣⲓ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲛⲉⲙ Ⲓⲱⲁⲕⲓⲙ ⲡⲉⲥϩⲁⲓ ⲛⲉⲙ ⲛⲉⲥⲥⲩⲅⲅⲉⲛⲏⲥ ⲧⲏⲣⲟⲩ ϫⲉ ⲙ̀ⲡⲟⲩϫⲉⲙ ⲟⲩϩⲱⲃ ⲉϥϣⲏϣ ⲉ̀ⲛⲉϩ ϧⲁ Ⲥⲟⲩⲥⲁⲛⲛⲁ ⲉϥϭⲓ ⲉ̀ϧⲟⲩⲛ ⲉ̀ⲣⲟⲥ. | Tsono Hilikiya ndi mkazi wake adathokoza Mulungu, nayenso mwamuna wake Yowakimu pamodzi ndi anansi onse aja adachita chimodzimodzi, poona kuti Suzana wapezeka wosalakwa. | ||||||||||||||
| 13:64 | And from that day onward Daniel had a great reputation among the people. | Ⲇⲁⲛⲓⲏⲗ ⲇⲉ ⲁϥⲉⲣ ⲟⲩⲛⲓϣϯ ⲙ̀ⲡⲉⲙ̀ⲑⲟ ⲙ̀ⲡⲓⲗⲁⲟⲥ ⲓⲥϫⲉⲛ ⲡⲓⲉ̀ϩⲟⲟⲩ ⲉⲧⲉⲙ̀ⲙⲁⲩ ⲛⲉⲙ ⲙⲉⲛⲉⲛⲥⲱϥ. | Ndiye kuyambira tsiku limenelo mpaka m'tsogolo mwake, Daniele ankamulemekeza kwambiri anthu onse. |